Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 7:7-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Ndipo Mose anali nazo zaka makumi asanu ndi atatu, ndi Aroni anali nazo zaka makumi asanu ndi atatu kudza zitatu, pamene ananena ndi Farao.

8. Ndipo Yehova ananena ndi Mose ndi Aroni, ndi kuti,

9. Pamene Farao adzalankhula nanu, ndi kuti, Dzicitireni codabwiza; pamenepo uzinena ndi Aroni, Tenga ndodo yako, Iponye pansi pamaso pa Farao, isanduke cinjoka,

10. Ndipo Mose ndi Aroni analowa kwa Farao, nacita monga momwe Yehova adawalamulira; ndipo Aroni anaponya pansi ndodo yace pamaso pa Farao, ndi pamaso pa anyamata ace, ndipo inasanduka cinjoka,

11. Pamenepo Farao anaitananso anzeru, ndi amatsenga; ndipo alembi a Aigupto, iwonso anacita momwemo ndi matsenga ao.

12. Pakuti yense anaponya pansi ndodo yace, ndipo zinasanduka zinjoka; koma ndodoya Aroni inameza ndodo zao,

13. Koma mtima wa Farao unalimba, ndipo sanamvera iwo; monga adalankhula Yehova.

14. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, Walemera mtima wa Farao, akana kulola anthu apite,

15. Muka kwa Farao m'mawa; taona, aturuka kumka kumadzi; nuime kumlinda m'mbali mwa nyanja; ndi ndodo idasanduka njokayo uigwire m'dzanja lako.

Werengani mutu wathunthu Eksodo 7