28. Ndipo Mose anauza Aroni mau onse a Yehova amene adamtuma nao, ndi zizindikilo zonse zimene adamlamulira.
29. Pamenepo Mose ndi Aroni anamuka nasonkhanitsa akuru onse a ana a Israyeli;
30. ndipo Aroni anawafotokozera mau onse amene Yehova adauza Mose, nacita zizindikilo zija pamaso pa anthu.
31. Ndipo anthuwo anakhulupirira; ndipo pamene anamva kuti Yehova adawazonda ana a Israyeli, ndi kuti adaona mazunzo ao, anawerama, nalambira Mulungu.