Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 4:28-31 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

28. Ndipo Mose anauza Aroni mau onse a Yehova amene adamtuma nao, ndi zizindikilo zonse zimene adamlamulira.

29. Pamenepo Mose ndi Aroni anamuka nasonkhanitsa akuru onse a ana a Israyeli;

30. ndipo Aroni anawafotokozera mau onse amene Yehova adauza Mose, nacita zizindikilo zija pamaso pa anthu.

31. Ndipo anthuwo anakhulupirira; ndipo pamene anamva kuti Yehova adawazonda ana a Israyeli, ndi kuti adaona mazunzo ao, anawerama, nalambira Mulungu.

Werengani mutu wathunthu Eksodo 4