Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 39:39-43 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

39. guwa la nsembe lamkuwa, ndi made ace amkuwa, mphiko zace, ndi zipangizo zace zonse, mkhate ndi tsinde lace;

40. nsaru zocingira za pabwalo, osici zace, ndi makamwa ace, ndi nsaru yotsekera pa cipata ca pabwalo, zingwe zace, ndi ziciri zace, ndi zipangizo zonse za nchito ya kacisi, za ku cihema cokomanako;

41. zobvala zokoma za kutumikira nazo m'malo opatulika, ndi zobvala zopatulika za Aroni wansembe, ndi zobvala za ana ace, kucita nazo nchito ya usembe.

42. Monga mwa zonse Yehova adamuuza Mose, momwemo ana a Israyeli anacita nchito zonse.

43. Ndipo Mose anaona nchito zonse, ndipo, taonani, adaicita monga Yehova adamuuza, momwemo adacita. Ndipo Mose anawadalitsa.

Werengani mutu wathunthu Eksodo 39