Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 39:11-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Ndi mzere waciwiri wa nofeki, safiri, ndi yahalomu.

12. Ndi mzere wacitatu wa lesemu, sibu, ndi akalama.

13. Ndi mzere wacinai wa tarisisi, sohamu, ndi yasefe; inakhala yogwirika ndi golidi maikidwe ace.

14. Ndipo miyalayi inakhala monga mwa maina a ana a Israyeli, khumi ndi awiri, monga mwa maina ao; ngati malocedwe a cosindikizira, yonse monga mwa maina ace, kwa mafuko khumi ndi awiriwo.

15. Ndipo anapangira pacapacifuwa maunyolo ngati zingwe, nchito yopota ya golidi woona.

16. Anapanganso zoikamo ziwiri zagolidi, ndi mphete ziwiri zagolidi; naika mphete ziwirizo pa nsonga ziwiri za capacifuwa.

Werengani mutu wathunthu Eksodo 39