Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 37:3-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Ndipo analiyengera mphete zinai zagolidi pa miyendo yace inai; mphete ziwiri pa mbali yace imodzi, ndi mphete: ziwiri pa mbali yace yina.

4. Ndipo anapanga mphiko za mtengo wasitimu, nazikuta ndi golidi.

5. Ndipo anapisa mphiko m'mphetezo pa mbali zace za likasalo, kuti anyamulire nazo likasa.

6. Ndipo anapanga cotetezerapo ca golidi woona; utali wace mikono iwiri ndi hafu, ndi kupingasa kwace mkono ndi hafu.

7. Anapanganso akerubi awiri agolidi; anacita kuwasula mapangidwe ace, pa mathungo ace swiri a coteteze rapo;

8. kerubi mmodzi pa mbali yace imodzi, ndi kerubi wilia pa mbali yace yina; anapanga akerubi ocokera m'cotetezerapo, pa mathungo ace awiri.

9. Ndipo akerubi anafunyulira mapiko ao m'mwamba, ndi kuphimba cotetezerapo ndi mao piko ao, ndi nkhope zao zopeoyana; zinapenya kucotetezerapo nkhope zao.

10. Ndipo anapanga gome la mtengo wasitimu; utali wace mikono iwiri, ndi kupingasa kwace mkono limodzi, ndi msinkhu wace mkono ndi hafu;

11. ndipo analikuta ndi golidi woona, nalipangira mkombero wagolidi pozungulira pace.

12. Analipangiranso mitanda pozungulirapo, yoyesa cikhato m'kupingasa kwace, ndi pamitanda pace pozungulira anapangirapo mkombero wagolidi.

13. Ndipo analiyengera mphete zinai zagolidi, naika mphetezo pa ngondya zace zinai zokhala pa miyendo yace inai.

14. Mphetezo zinali pafupi pa mitanda, zikhale zopisamo mphiko kunyamulira nazo gomelo.

15. Ndipo anapanga mphiko za mtengo wasitimu, nazikuta ndigolidi, kunyamulira nazo gomelo.

16. Anapanganso zipangizo za gomelo, mbale zace, ndi zipande zace, ndi mitsuko yace, ndi zikho zace zakuthira nazo, za golidi woona.

17. Ndipo anapanga coikapo nyali ca golidi woona; mapangidwe ace a coikapo nyalico anacita cosula, tsinde lace ndi thupi lace, zikho zace, mitu yace, ndi maluwa ace zinakhala zocokera m'mwemo;

Werengani mutu wathunthu Eksodo 37