Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 37:20-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. Ndipo pa coikapo nyali comwe panali zikho zinai zopangika ngati katungurume, mitu yace ndi maluwa ace;

21. ndipo panali mutu pansi pa mphanda ziwiri, zoturuka m'mwemo, ndi mutu pansi pa mphanda ziwiri, zoturuka m'mweno, ndi mutu pansi pa mphanda ziwiri, zoturuka m'mwemo, inatero pa mphanda zisanu ndi imodzi zocokera m'mwemo.

22. Mitu yao ndi mphanda zao zinaturuka m'mwemo; conseci cinali cosulika pamodzi ca golidi woona.

23. Ndipo anapanga nyali zace zisanu ndi ziwiri ndi mbano zace, ndi zoolera zace, za golidi woona.

24. Anacipanga ici ndi zipangizo zace zonse za talente wa golidi woona.

25. Ndipo anapanga guwa la nsembe lofukizapo la mtengo wasitimu; utali wace mkono, ndi kupingasa kwace mkono, lampwamphwa; ndimsinkhu wace mikono iwiri; nyanga zace zinaturuka m'mwemo.

26. Ndipo analikuta ndi golidi woona, pamwamba pace, ndi mbali zace pozungulira, ndi nyanga zace; ndipo analipangira mkombero wagolidi pozungulira pace.

27. Ndipo analipangira mphete ziwiri zagolidi pansi pa mkombero wace, pa ngondya zace ziwiri, pa mbali zace ziwiri, zikhale zopisamo mphiko kulinyamulira nazo.

28. Ndipo anazipanga mphiko za mtengo wasitimu, nazikuta ndi golidi.

29. Anapanganso mafuta opatulika akudzoza nao, ndi cofukiza coona ca pfungo lokoma, mwa macitidwe a wosanganiza.

Werengani mutu wathunthu Eksodo 37