1. Ndipo Bezaleli anapanga likasa la mtengo wasitimu; utali wace mikono iwiri ndi hafu, ndi kupingasa kwace mkono ndi hafu, ndi msinkhu wace mkono ndi hafu;
2. ndipo analikuta ndi golidi woona m'kati ndi kunja, nalipangira mkombero wagolidi pozungulira pace.
3. Ndipo analiyengera mphete zinai zagolidi pa miyendo yace inai; mphete ziwiri pa mbali yace imodzi, ndi mphete: ziwiri pa mbali yace yina.
4. Ndipo anapanga mphiko za mtengo wasitimu, nazikuta ndi golidi.