Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 37:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo Bezaleli anapanga likasa la mtengo wasitimu; utali wace mikono iwiri ndi hafu, ndi kupingasa kwace mkono ndi hafu, ndi msinkhu wace mkono ndi hafu;

2. ndipo analikuta ndi golidi woona m'kati ndi kunja, nalipangira mkombero wagolidi pozungulira pace.

3. Ndipo analiyengera mphete zinai zagolidi pa miyendo yace inai; mphete ziwiri pa mbali yace imodzi, ndi mphete: ziwiri pa mbali yace yina.

4. Ndipo anapanga mphiko za mtengo wasitimu, nazikuta ndi golidi.

Werengani mutu wathunthu Eksodo 37