Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 36:21-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Utali wace wa thabwa limodzi ndiwo mikono khumi, ndi kupingasa kwace kwa thabwa limodzi ndiko mkono ndi hafu.

22. Pa thabwa limodzi panakhala mitsukwa iwiri, yomangika pamodzi; anawapanga momwemo matabwa onse a kacisi.

23. Ndipo anapanga matabwa a kacisi; matabwa makumi awiri a ku mbali ya kumwela, kumwela;

24. napanga makamwa makumi anai pansi pamatabwa makumi awiri; makamwa awiri pansi pa thabwa limodzi kwa mitsukwa yace iwiri, ndi makamwa awiri pansi pa thabwa lina kwa mitsukwa yace iwiri.

Werengani mutu wathunthu Eksodo 36