18. Ndipo anapanga zokowera makumi asanu zamkuwa kumanga pamodzi hemalo, kuti likhale limodzi.
19. Ndipo anasokera hemalo cophimba ca zikopa za nkhosa zamphongo zonika zofiira, ndi cophimba ca zikopa za akatumbu pamwamba pace.
20. Ndipo anapanga matabwa a kacisi, oimirika, a mtengo wasitimu.