33. ndi kuzokota miyala voikika, ndi kuzokota mitengo, kucita m'nchito ziri zonse zaluso.
34. Ndipo anaika m'mtima mwace kuti alangize ena, iye ndi Aholiabu mwana wa Ahisama, wa pfuko la Dani.
35. Amenewo anawadzaza ndi luso lamtima, lakucita nchito ziri zonse, ya kuzokota miyala, ndi ya mmisiri waluso, ndi ya wopikula ndi lamadzi ndi lofiirira, ndi lofiira, ndi bafuta wa thonje losansitsa, ndi ya muomba, ya iwo akucita nchito iri yonse, ndi ya iwo olingirira nchito yaluso.