18. Ndipo anati, Ndionetsenitu ulemerero wanu.
19. Ndipo iye anati, Ndidzapititsa ukoma wanga wonse pamaso pako, ndipo ndidzachula dzina la Yehova pamaso pako; ndipo ndidzacitira ufulu amene ndidzamcitira ufulu; ndi kucitira cifundo amene ndidzamcitira cifundo.
20. Ananenanso, Sungathe kuona nkhope yanga; pakuti palibe munthu adzandiona Ine ndi kukhala ndi moyo.
21. Ndipo Yehova anati, Taona pali Inepo pali malo, ndipo uime pathanthwe;
22. ndipo kudzakhala, pakupitira olemerero wanga, ndidzakuika mu mpata wa thanthwe, ndi kukuphimba ndi dzanja langa, mpaka nditapitira;
23. ndipo pamene ndicotsa dzanja langa udzaona m'mbuyo mwanga; koma nkhope yanga siidzaoneka.