Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 31:15-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Agwire nchito masiku asanu ndi limodzi; koma lacisanu ndi ciwiri ndilo Sabata lakupumula, lopatulika la Yehova; ali yense wogwira nchito tsiku la Sabata aphedwe ndithu.

16. Cifukwa cace ana a Israyeli azisunga Sabata, kucita Sabata mwa mibadwo yao, likhale pangano losatha;

17. ndico cizindikilo cosatha pakati pa Ine ndi ana a Israyeli; pakuti Yehova analenga zam'mwamba ndi dziko lapansi masiku asanu ndi limodzi, napumula tsiku lacisanu ndi ciwiri, naonanso mphamvu.

18. Ndipo atatha iye kulankhula ndi Mose, pa phiri la Sinai, anampatsa magome awiri a mboni, magome amiyala, olembedwa ndi cala ca Mulungu.

Werengani mutu wathunthu Eksodo 31