Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 26:22-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

22. Ndipo uzipanga matabwa asanu ndi limodzi kwa mbali ya kacisi ya kumbuyo kumadzulo.

23. Nupange matabwa awiri a ngondya za kacisi za kumbuyo.

24. Ndipo akhale ophatikizika pamodzi patsinde, nakhalenso ophatikizika pamodzi kumutu kwace ndi mphete imodzi; azitero onse awiri; azikhala a ngondya ziwiri.

25. Ndipo pakhale matabwa asanu ndi atatu, ndi makamwa ao asiliva, ndiwo makamwa khumi mphambu asanu ndi limodzi; makamwa awiri pansi pa thabwa limodzi, ndi makamwa awiri pansi pa thabwa lina.

26. Ndipo uzipanga mitanda ya mtengo wasitimu; isanu ya matabwa a pa mbali yina ya kacisi,

27. ndi mitanda isanu ya matabwa a Pel mbali yina ya kacisi, ndi mitanda isanu ya matabwa a pa mbali ya kacisi ya kumbuyo kumadzulo.

Werengani mutu wathunthu Eksodo 26