Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 26:10-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Ndipo uziika magango makumi asanu m'mphepete mwa nsaru imodzi, ya kuthungo ya cilumikizano, ndi magango makumi asanu m'mphepete mwa nsaru ya kuthungo ya cilumikizano cina.

11. Ndipo uzipanga zokowera makumi asanu zamkuwa, ndi kukowetsa zokowerazo m'magangomo, ndi kumanga pamodzi hemalo likhale limodzi.

12. Ndipo cotsalaco pa nsaru za hemalo, hafu yace ya nsaru yotsalirayo, icinge pambuyo pace pa kacisi.

13. Ndi mkono wa pa mbali yino, ndi mkono wa pa mbali inzace, wakutsalira m'utali wace wa nsaru za hemalo, icinge pambali zace za kacisi, mbali yino ndi mbali yina, kumphimba.

14. Ndipo uzipangira hema cophimba ca zikopa za nkhosa zamphongo zonika zofiira, ndi cophimba za zikopa za akatumbu pamwamba pace.

15. Ndipo uzipangira kacisi matabwa oimirika, a mtengo wasitimu.

16. Utali wace wa thabwa limodzi ndiwo mikono khumi, ndi kupingasa kwace kwa thabwali mkono ndi hafu.

17. Pa thabwa limodzi pakhale mitsukwa iwiri, yomangika pamodzi; uzitero pa matabwa onse a kacisi.

18. Ndipo uzipanga matabwa a kacisi, matabwa makumi awiri ku mbali ya kumwela, kumwela.

19. Nuzipanga makamwa makumi anai asiliva pansi pa matabwa makumi awiri; makamwa awiri pansi pa thabwa limodzi kwa mitsukwa yace iwiri, ndi makamwa awiri pansi pa thabwa lina kwa mitsukwa yace iwiri;

20. ndi pa mbali yace yina ya kacisi, mbali ya kumpoto, pakhale matabwa makumi awiri; ndi makamwa asiliva makumi anai;

Werengani mutu wathunthu Eksodo 26