Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 23:29-33 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

29. Sindidzawaingista pamaso pako caka cimodzi; kuti dziko lingakhale bwinja, ndi zirombo za kuthengo zingakucurukire.

30. Ndidzawaingitsa pang'ono pang'ono pamaso pako, kufikira utacuruka, ndi kulandira dziko colowa cako.

31. Ndipo ndidzalemba malire ako kuyambira ku Nyanja Yofiira, kufikira ku nyanja ya Afilisiti, ndi kuyambira kucipululu kufikira ku Nyanja; popeza ndidzapereka okhala m'dzikolo m'dzanja lako, ndipo uziwaingitsa pamaso pako.

32. Usapangana nao, kapena ndi milungu yao.

33. Asakhale m'dziko lako iwowa, kuti angakulakwitse pa loe; pakuti ukatumikira milungu yao, kudzakukhalira msampha ndithu.

Werengani mutu wathunthu Eksodo 23