Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 23:1-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Usatola mbiri yopanda pace; usathandizana naye woipa ndi kukhala mboni yocititsa ciwawa.

2. Usatsata unyinji wa anthu kucita coipa; kapena usacita umboni kumlandu, ndi kupatukira kutsata unyinji ndi kukhotetsa mlandu;

3. kapena usakometsera munthu wosauka pa mlandu wace.

4. Ukakomana ndi ng'ombe kapena buru wa mdani wako zirimkusokera, uzimbwezera izo ndithu.

5. Ukaona buru wa munthuwakudana nawe alikugona pansi ndi katundu wace, ndipo ukadaleka kuthandiza, koma uzimthandiza ndithu.

6. Usakhotetsa mlandu wa mnzako waumphawi.

7. Uzikhala kutali ndi mlandu wonama; ndipo usapha munthu wosacimwa ndi wolungama; pakuti sindidzayesa wolungama munthu woipa.

8. Usalandira cokometsera mlandu; pakuti cokometsera mlandu cidetsa maso a openya, nicisanduliza mlandu wa olungama,

9. Usampsinia mlendo; pakuti mudziwa mtima wa mlendo popeza munali alendo m'dziko la Aigupto.

10. Ndipo uzibzala m'munda mwako zaka zisanu ndi cimodzi, ndi kututa zipatso zako;

Werengani mutu wathunthu Eksodo 23