Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 22:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Munthu akaba ng'ombe, kapena nkhosa, nakaipha, kapena kuigulitsa, azilipa ng'ombe zisanu pa ng'ombeyo; ndi nkhosa zinai pa nkhosayo,

2. Akampeza wakuba alimkuboola, nakamkantha kotero kuti wafa, palibe camwazi.

3. Litamturukira dzuwa, pali camwazi; wakubayo azilipa ndithu; ngati alibe kanthu, amgulitse pa umbala wace.

4. Akacipeza cakubaco ciri m'dzanja lace camoyo, ngakhale ng'ombe, kapena buru, kapena nkhosa, alipe mowirikiza.

Werengani mutu wathunthu Eksodo 22