Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 21:7-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Ndipo munthu akagulitsa mwana wace wamkazi akhale mdzakazi, iyeyo asaturuke monga amaturuka anyamata.

8. Akapanda kumkonda mbuye wace, amene anamtoma mwini yekha, azilola kuti amuombole; alibe mphamvu yakumgulitsa kwa anthu acilendo, popeza wacita naye monyenga.

9. Koma ngati amtomera mwana wace wamwamuna, amcitire monga kuyenera ana akazi.

10. Akamtengera mkazi wina, asacepetse cakudya cace, zobvala zace, ndi za ukwati zace zace.

11. Ndipo akapanda kumcitira izi zitatu, azituruka cabe, osaperekapo ndalama.

12. Iye amene akantha munthu kotero kuti wafa, aphedwe ndithu.

13. Koma akapanda kumlalira, koma Mulungu akalola akomane ndi mnzace, ndidzakuikirani pothawirapo iye.

14. Koma munthu akacita dala pa mnzace, kumupha monyenga; uzimcotsa ku guwa langa la nsembe, kuti afe.

15. Munthuwakukanthaatatewace, kapena amai wace, aphedwe ndithu.

16. Iye wakuba munthu, angakhale wamgulitsa, kapena akampeza m'dzanja lace, aphedwe ndithu.

17. Munthu wakutemberera atate wace, kapena amai wace, aphedwe ndithu.

18. Akalimbana amuna, ndipo wina akakantha mnzace ndi mwala, kapena ndi nkhonyo, wosafa iye, koma wakhulungira pakama;

19. akaukanso, nakayendayenda pabwalo ndi ndodo yace, womkanthayo azikhala womasuka; pakutsotsa pace pokha azimbwezera, namcizitse konse.

20. Munthu akakantha mnyamata wace, kapena mdzakazi wace, ndi ndodo, ndipo akafa padzanja pace; ameneyo aliridwe ndithu.

21. Koma akakhala wosafa tsiku limodzi kapena awiri, asalirike, pakuti ndiye ndalama ya mbuye wace.

22. Akayambana amuna, nakakantha mkazi ali ndi pakati, kotero kuti abala, koma alibe kuphwetekwa; alipe ndithu, monga momwe amchulira mwamuna wa mkaziyo; apereke monga anena oweruza.

23. Koma ngati kuphweteka kukalipo, uzipereka moyo kulipa moyo,

24. diso kulipa diso, dzino kulipa dzino, dzanja kulipa dzanja, phazi kulipa phazi,

Werengani mutu wathunthu Eksodo 21