31. Ingakhale yatunga mwana wamwamuna kapena wamkazi, aicitire monga mwa ciweruzo ici.
32. Ng'ombeyo ikatunga mnyamata kapena mdzakazi, azipatsa mbuye wace ndalama za masekele a siliva makumi atatu, ndipo ng'ombeyo aiponye miyala.
33. Munthu akafukula dzenje, kapena akakumba dzenje, osalibvundikira, ndipo ikagwamo ng'ombe kapena buru,
34. mwini dzenje azilipa; azilipa ndalama kwa mwini nyamayo, koma yakufayo ndi yace.
35. Ng'ombe ya mwini ikapweteka ng'ombe ya mnzace, nifa, azigulitsa ng'ombe yamoyoyo, nagawe ndalama zace; naigawe, ndi yakufa yomweyo.