Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 19:18-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Ndipo phiri la Sinai linafuka monsemo, popeza Yehova anatsikira m'moto pamenepo; ndi utsi wace unakwera ngati utsi wa m'ng'anjo, ndi phiri lonse linagwedezeka kwambiri,

19. Ndipo pamene liu la lipenga linamveka linakulira-kulira, Mose ananena, ndi Mulungu anamyankha ndi mau.

20. Ndipo Yehova anatsikira pa phiri la Sinai, pamutu pace pa phiri; ndipo Yehova anaitana Mose akwere pamutu pa phiri; ndi Mose anakwerapo.

21. Ndipo Yehova anati kwa Mose, Tsika, cenjeza anthu, kuti angapyolere kwa Yehova kudzaona, ndipo angagwe ambiri a iwowa.

22. Ansembenso, akuyandikiza kwa Yehova adzipatulitse, angawapasule Yehova.

23. Ndipo Mose anati kwa Yehova, Anthu sangathe kukwera m'phiri la Sinai; pakuti Inu mwaticenjeza, ndi kuti, Lemba malire m'phirimo, ndi kulipatula.

24. Ndipo Yehova anati kwa iye, Muka, tsika: nukwere iwe ndi Aroni pamodzi ndi iwe; koma ansembe ndi anthu asapyole kukwera kwa Yehova, angawapasule.

25. Pamenepo Mose anawatsikira anthu, nanena nao.

Werengani mutu wathunthu Eksodo 19