Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 15:9-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Mdani anati,Ndiwalondola, ndiwakumika, ndidzagawa zofunkha;Ndidzakhuta nao mtima;Ndidzasolola lupanga langa, dzanja langa lidzawaononga.

10. Munaombetsa mphepo yanu, nyanja inawamiza;Anamira m'madzi akuru ngati mtobvu.

11. Manana ndi Inu ndani mwa milungu, Yehova?Manana ndi Inu ndani, wolemekezedwa, woyera,Woopsa pomyamika, wakucita zozizwa?

12. Mwatambasula dzanja lanu lamanja,Nthaka inawameza,

13. Mwa cifundo canu mwatsogolera anthu amene mudawaombola;Mwa mphamvu yanu mudawalondolera njira yakumka pokhala panu poyera.

14. Mitundu ya anthu idamva, inanthunthumira;Kuda mtima kwagwira anthu okhala m'Filistiya.

15. Pamenepo mafumu a Edomu anadabwa;Agwidwa nako kunthunthumira amphamvu a ku Moabu;Okhala m'Kanani onse asungunukamtima.

16. Kuopa kwakukuru ndi mantha ziwagwera;Pa dzanja lanu lalikuru akhala cete ngati mwala;Kufikira apita anthu anu, Yehova,Kufikira apita anthu amene mudawaombola.

17. Mudzawafikitsa, ndi kuwaoka pa phiri la colowa canu,Pamalo pamene munadzipangira mukhalepo, Yehova,Malo oyera, amene manja anu, Ambuye, adakhazikika.

Werengani mutu wathunthu Eksodo 15