Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 13:18-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Koma Mulungu anawazungulitsa anthuwo, ku njira ya kucipululu ya Nyanja Yofiira; ndipo ana a Israyeli anakwera kucokera m'dziko la Aigupto okonzeka.

19. Ndipo Mose anamuka nao mafupa a Yosefe; pakuti adawalumbiritsatu ana a Israyeli ndi kuti, Mulungu adzakuzondani ndithu ndipo mukakwere nao mafupa anga osawwya kuno.

20. Ndipo anacokera ku Sukoti, nagona ku Etamu, pa malekezero a cipululu.

21. Ndipo Yehova anawatsogolera usana ndi mtambo njo kuwatsogolera m'njira; ndi usiku ndi moto njo, wakuwawalitsira; kuti ayende usana ndi usiku;

22. sanacotsa mtambo usana, kapena mtambo wamoto usiku, pamaso pa anthu.

Werengani mutu wathunthu Eksodo 13