Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Eksodo 12:23-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

23. Pakuti Yehova adzapita pakatipo kukantha Aaigupto; koma pamene adzaona mwaziwo pa mphuthu pamwamba ndi za pambali, Yehova adzapitirira pakhomopo, osalola woonongaalowe m'nyumba zanu kukukanthani.

24. Ndipo muzisunga cinthu ici cikhale lemba la kwa inu, ndi kwa ana anu ku nthawi zonse.

25. Ndipo kudzakhala, pamene mulowa m'dziko limene Yehova adzakupatsani, mensa analankhula, muzisunga kutumikira kumeneku.

26. Ndipo kudzakhala, pamene ana anu adzanena ndi inu, Kutumikiraku muli nako nkutani?

Werengani mutu wathunthu Eksodo 12