Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 4:35-43 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

35. Inu munaciona ici, kuti mudziwe kuti Yehova ndiye Mulungu; palibe wina wopanda iye.

36. Anakumvetsani mau ace kucokera kumwamba, kuti akuphunzitseni; ndipo pa dziko lapansi anakuonetsani moto wace waukuru; nimunamva mau ace pakati pa moto.

37. Ndipo popeza anakonda makolo anu, anasankha mbeu zao zakuwatsata, nakuturutsani pamaso pace ndi mphamvu yace yaikuru, m'Aigupto;

38. kupitikitsa amitundu akuru ndi amphamvu oposa inu pamaso panu, kukulowetsani ndi kukupatsani dziko lao likhale colowa canu, monga lero lino.

39. Potero dziwani lero tino nimukumbukire m'mtima mwanu, kuti Yehova ndiye Mulungu, m'thambo la kumwamba ndi pa dziko lapansi; palibe wina.

40. Muzisunga malemba ace, ndi malamulo ace, amene ndikuzuzani lero lino, kuti cikukomereni inu ndi ana anu akukutsatani, ndi kuti masiku anu acuruke pa dziko limene Yehova Mulungu wanu akupatsani likhale lanu kosatha.

41. Pamenepo Mose anapatula midzi itatu tsidya lija la Yordano loturuka dzuwa;

42. kuti athawireko wakupha munthu, osamupha mnansi wace dala, osamkwiyira ndi kale lonse; ndi kuti, akathawira ku umodzi wa midzi iyi, akhale ndi moyo:

43. ndiyo Bezere, m'cipululu, m'dziko lacidikha, ndiwo wa Anrubeni; ndi Ramoti m'Gileadi, ndiwo wa Agadi; ndi Golani, m'Basana, ndiwo wa Amanase.

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 4