Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 4:34-37 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

34. Kapena kodi anayesa Mulungu kumuka ndi kudzitengera mtundu mwa mtundu wina wa anthu, ndi mayesero, ndi zizindikilo, ndi zozizwa, ndi nkhondo, ndi mwa dzanja lamphamvu, ndi mkono wotambasuka, ndi mwa zoopsa zazikuru, monga mwa zonse Yehova Mulungu wanu anakucitirani m'Aigupto pamaso panu?

35. Inu munaciona ici, kuti mudziwe kuti Yehova ndiye Mulungu; palibe wina wopanda iye.

36. Anakumvetsani mau ace kucokera kumwamba, kuti akuphunzitseni; ndipo pa dziko lapansi anakuonetsani moto wace waukuru; nimunamva mau ace pakati pa moto.

37. Ndipo popeza anakonda makolo anu, anasankha mbeu zao zakuwatsata, nakuturutsani pamaso pace ndi mphamvu yace yaikuru, m'Aigupto;

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 4