Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 33:24-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

24. Ndi za Aseri anati,Aseri adalitsidwe mwa anawo;Akhale wobvomerezeka mwa abale ace,Abviike phazi lace m'mafuta.

25. Nsapato zako zikhale za citsulo ndi mkuwa;Ndipo monga masiku ako momwemo mphamvu yako.

26. Palibe wina ngati Mulungu, Yesuruni iwe,Wakuyenda wokwera pathambo, kukuthandiza,Ndi pa mitambo m'ukulu wace.

27. Mulungu wamuyaya ndiye mokhaliramo mwako;Ndi pansipo pali manja osatha.Ndipo aingitsa mdani pamaso pako,Nati, Ononga.

28. Ndipo Israyeli akhala mokhazikika pa yekha;Kasupe wa Yakobo;Akhala m'dziko la tirigu ndi vinyo;Inde thambo lace likukha mame.

29. Wodala iwe, Israyeli;Akunga iwe ndani, mtundu wa anthu opulumutsidwa ndi Yehova,Ndiye cikopa ca thandizo lako,Iye amene akhala lupanga la ukulu wako!Ndi adani ako adzakugonjera; Ndipo udzaponda pa misanje yao.

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 33