Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 32:34-47 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

34. Kodi sicisungika ndi Ine,Colembedwa cizindikilo mwa cuma canga ceni ceni?

35. Kubwezera cilango nkwanga, kubwezera komwe,Pa nyengo ya kuterereka phazi lao;Pakuti tsiku la tsoka lao layandika,Ndi zinthu zowakonzeratu zifulomira kudza.

36. Popeza Yehova adzaweruza anthuace,Nadzacitira nsoni anthu ace;Pakuona iye kuti mphamvu yao yatha,Wosatsala womangika kapena waufulu,

37. Pamenepo adzati, Iri kuti milunguyao,Thanthwe limene anathawirako?

38. Imene inadya mafuta a nsembe zao zophera,Nimwa vinyo wa nsembe yao yothira?Iuke nikuthandizeni, Ikhale pobisalapo panu.

39. Tapenyani tsopano kuti Ine ndine iye,Ndipo palibe mulungu koma Ine;Ndipha Ine, ndikhalitsanso ndi mayo:Ndikantha, ndicizanso Ine;Ndipo palibe wakulanditsa m'dzanja langa.

40. Pakuti ndikweza dzanja langa kuloza kumwamba,Ndipo nditi, Pali moyo wanga kosatha,

41. Ndikanola lupanga langa lonyezimira,Ndi dzanja langa likagwira ciweruzo;Ndidzabwezera cilango ondiukira,Ndi kulanga ondida.

42. Mibvi yanga ndiiledzeretsa nao mwazi,Ndi lupanga langa lidzalusira nyama;Ndi mwazi wa ophedwa ndi ogwidwa,Ndi mutu wacitsitsi wa mdani,

43. Kondwerani, amitundu inu, ndi anthu ace;Adzalipsira mwazi wa atumiki ace,Adzabwezera cilango akumuukira,Nadzafafanizira zoipa dziko lace, ndi anthu ace.

44. Ndipo anadza Mose nanena mau onse a nyimbo iyi m'makutu mwa anthu, iye, ndi Hoseya mwana wa Nuni.

45. Ndipo Mose anatha kunena mau awa onse kwa Israyeli wonse;

46. nati nao, Ikani mitima yanu pa mau onse ndikucitirani nao mboni lero; kuti muuze ana anu asamalire kuwacita mau onse a cilamulo ici.

47. Pakuti sicikhala kwa inu cinthu copanda pace, popeza ndico moyo wanu, ndipo mwa cinthu ici mudzacurukitsa masiku anu m'dziko limene muolokera Yordano, kulilandira.

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 32