Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 32:30-40 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

30. Mmodzi akadapitikitsa zikwi,Awiri akadathawitsa zikwi khumi,Akadapanda kuwagulitsa Thanthwelao,Akadapanda kuwapereka Yehova.

31. Popeza thanthwe lao nlosanga Thanthwe lathu,Oweruza a pamenepo ndiwo adani athu.

32. Pakuti mpesa wao ndiwo wa ku Sodomu,Ndi wa m'minda ya ku Gomora;Mphesa zao ndizo mphesa zandulu,Matsangwi ao ngowawa.

33. Vinyo wao ndiwo ululu wa zinjoka,Ndi ululu waukali wa mphiri.

34. Kodi sicisungika ndi Ine,Colembedwa cizindikilo mwa cuma canga ceni ceni?

35. Kubwezera cilango nkwanga, kubwezera komwe,Pa nyengo ya kuterereka phazi lao;Pakuti tsiku la tsoka lao layandika,Ndi zinthu zowakonzeratu zifulomira kudza.

36. Popeza Yehova adzaweruza anthuace,Nadzacitira nsoni anthu ace;Pakuona iye kuti mphamvu yao yatha,Wosatsala womangika kapena waufulu,

37. Pamenepo adzati, Iri kuti milunguyao,Thanthwe limene anathawirako?

38. Imene inadya mafuta a nsembe zao zophera,Nimwa vinyo wa nsembe yao yothira?Iuke nikuthandizeni, Ikhale pobisalapo panu.

39. Tapenyani tsopano kuti Ine ndine iye,Ndipo palibe mulungu koma Ine;Ndipha Ine, ndikhalitsanso ndi mayo:Ndikantha, ndicizanso Ine;Ndipo palibe wakulanditsa m'dzanja langa.

40. Pakuti ndikweza dzanja langa kuloza kumwamba,Ndipo nditi, Pali moyo wanga kosatha,

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 32