Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 30:2-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. nimukabwerera kwa Yehova Mulungu wanu, ndi kumvera mali ace, monga mwa zonse ndikuuzani lero lino, inu ndi ana anu, ndi mtima wanu wonse, ndi moyo wanu wonse;

3. pamenepo Yehova Mulungu wanu adzaucotsa ukapolo wanu, ndi kukucitirani cifundo; nadzabwera ndi kukumemezani mwa mitundu yonse ya anthu, kumene Yehova Mulungu wanu anakubalalitsiraniko.

4. Otayika anu akakhala ku malekezero a thambo, Yehova Mulungu wanu adzakumemezani kumeneko, nadzakutenganiko;

5. ndipo Yehova Mulungu wanu adzakulowetsani m'dziko lidakhala lao lao la makolo anu, nilidzakhala lanu lanu; ndipo adzakucitirani zokoma, ndi kukucurukitsani koposa makolo anu.

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 30