Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 3:12-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Ndipo dziko ili tinalilanda muja; kuyambira ku Aroeri, wa ku mtsinje wa Arinoni, ndi dera lina la ku mapiri a Gileadi, ndi midzi yace, ndinapatsa Arubeni ndi Agadi.

13. Ndi cotsalira ca Gileadi, ndi Basana lonse, dziko la Ogi, ndinapatsa pfuko la hafu la Manase; dziko lonse la Arigobi, pamodzi ndi Basana. (Ndilo lochedwa dziko la Arefai.

14. Yairi mwana wa Manase analanda dziko lonse la Arigobi, kufikira malire a Agesuri ndi Amaakati; nalicha dzina lace, Basana Haroti Yairi, kufikira lero lino.)

15. Ndipo ndinampatsa Makiri Gileadi.

16. Koma ndinapatsa Arubeni ndi Agadi kuyambira ku Gileadi kufikira ku mtsinje wa Arinoni, pakati pa cigwa ndi malire ace, kufikira mtsinje wa Yaboki, ndiwo malire a ana a Amoni;

17. ndi cidikha, ndi Yordano ndi malire ace, kuyambira ku Kinerete kufikira ku nyanja ya kucidikha, ndiyo Nyanja ya Mcere, patsinde pa Pisiga, kum'mawa.

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 3