Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 3:1-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Pamenepo tinatembenuka, ndi kubwera kumka njira ya ku Basana; ndipo Ogi mfumu ya Basana anaturuka kukomana nafe, kugwirana nafe nkhondo, iye ndi anthu ace onse, ku Edrei.

2. Ndipo Yehova anati kwa ine, Usamuopa; popeza ndampereka iye ndi anthu ace onse, ndi dziko lace, m'dzanja lako; umcitire monga umo unacitira Sihoni mfumu ya Aamori, amene anakhala m'Hesiboni.

3. Potero Yehova Mulungu wathu anaperekanso m'manja mwathu Ogi mfumu ya Basana, ndi anthu ace onse, ndipo tinamkantha kufikira sanamtsalira ndi mmodzi yense.

4. Ndipo muja tinalanda midzi yace yonse; kunalibe mudzi sitinaulanda m'manja mwao, midzi makumi asanu ndi limodzi, dera lonse la Arigobi, dziko la Ogi m'Basana.

5. Yonseyi ndiyo midzi yozinga ndi malinga atali, zitseko, ndi mipiringidzo; pamodzi ndi midzi yambirimbiri yopanda malinga.

6. Ndipo tinaiononga konse, monga umo tinacitira Sihoni mfumu ya Hesiboni, ndi kuononga konse midzi yonse, amuna, akazi ndi ana.

7. Koma zoweta zonse ndi zofunkha za m'midzi, tinadzifunkhira tokha.

8. Ndipo muja tinalanda dziko m'manja mwa mafumu awiri a Aamori okhala tsidya lija la Yordano, kuyambira mtsinje wa Arinoni kufikira phiri la Herimoni;

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 3