Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 29:24-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

24. inde amitundu onse adzati, Yehova anacitira dziko ili cotero cifukwa ninji? nciani kupsa mtima kwakukuru kumene?

25. Pamenepo adzati, Popeza analeka cipangano ca Yehova, Mulungu wa makolo ao, cimene anacita nao pakuwaturutsa m'dziko la Aigupto;

26. napita natumikira milungu yina, naigwadira, milungu imene sanaidziwa, imene sanawagawira;

27. cifukwa cace Mulungu anapsera mtima dziko ili kulitengera temberero lonse lolembedwa m'buku ili.

28. Ndipo Yehova anawazula m'nthaka mwao mokwiya ndi mozaza, ndi m'ukali waukuru, nawaponya m'dziko lina, monga lero lino.

29. Zinsinsi nza Yehova Mulungu wathu; koma zobvumbuluka nza ife ndi ana athu kosatha, kuti ticite mau onse a cilamulo ici.

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 29