Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 29:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Awa ndi mau a cipangano cimene Yehova analamulira Mose acicite ndi ana a Israyeli m'dziko la Moabu, pamodzi ndi cipanganoco anacita nao m'Horebe.

2. Ndipo Mose anaitana Israyeli wonse, nati nao, Munapenya inu zonse zimene Yehova anacitira Farao, ndi anyamata ace onse, ndi dziko lace lonse, pamaso panu m'dziko la Aigupto;

3. mayesero akuruwa maso anu anawapenya, zizindikilozo, ndi zozizwa zazikuru zija;

4. koma Yehova sanakupatsani mtima wakudziwa, ndi maso akupenya, ndi makutu akumva, kufikira lero lino.

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 29