Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 27:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo Mose ndi akuru a Israyeli anauza anthu, nati, Sungani malamulo onse ndikuuzani lero.

2. Ndipo kudzali, tsiku lakuoloka inu Yordano kulowa dziko limene Yehova Mulungu wanu akupatsani, kuti mudziutsire miyala yaikuru, ndi kuimata ndi njeresa;

3. ndipo mulemberepo mau onse a cilamulo ici, mutaoloka; kuti mulowe m'dziko limene Yehova Mulungu wanu akupatsani, dziko moyenda mkaka ndi uci ngati madzi, monga Yehova Mulungu wa makolo anu ananena ndi inu.

4. Ndipo kudzali, mutaoloka Yordano, muutse miyala iyi ndikuuzani lero, m'phiri la Ebala, ndi kuimata ndi njeresa.

5. Ndipo komweko mumangire Yehova Mulungu wanu guwa la nsembe, guwa la nsembe lamiyala; musakwezepo cipangizo cacitsulo.

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 27