Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 25:10-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Ndipo azimucha dzina lace m'Israyeli, Nyumba ya uje anamcotsa nsapato.

11. Akalimbana wina ndi mnzace, nakayandikiza mkazi wa winayo kulanditsa mwamuna wace m'dzanja la wompandayo, nakaturutsa dzanja lace, ndi kumgwira kudzibvalo;

12. pamenepo muzidula dzanja lace; diso lanu lisamcitire cifundo.

13. Musamakhala nayo m'thumba mwanu miyala ya miyeso iwiri, waukuru ndi waung'ono.

14. Musamakhala nayo m'nyumba yanu miyeso ya efa yosiyana, waukuru ndi waung'ono.

15. Muzikhala nao mwala wa muyeso wofikira ndi woyenera; mukhale nao muyeso wa efa wofikira ndi woyenera; kuti masiku anu acuruke m'dziko limene Yehova Mulungu wanu akupatsani.

16. Pakuti onse akucita zinthu izi, onse akucita cisalungamo, Yehova Mulungu wanu anyansidwa nao.

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 25