Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 23:8-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Ana obadwa nao a mbadwo wacitatu alowe m'msonkhano wa Yehova.

9. Nkhondo yanu ikaturuka pa adani anu, mudzisunge kusacita coipa ciri conse.

10. Pakakhala munthu pakati pa inu, ndiye wosayera cifukwa cocitika usiku, azituruka kunja kwa cigono, asalowe pakati pa cigono;

11. koma kudzali pofika madzulo, asambe m'madzi; ndipo litalowa dzuwa alowe pakati pa cigono.

12. Mukhale nao malo kunja kwa cigono kumene muzimukako kuthengo;

13. nimukhale naco cokumbira mwa zida zanu; ndipo kudzali, pakukhala inu pansi kuthengo mukumbe naco, ndi kutembenuka ndi kufotsera cakuturukaco;

14. popeza Yehova Mulungu wanu ayenda pakati pa cigono canu, kukupulumutsani ndi kupereka adani anu pamaso panu; cifukwa cace cigono canu cikhale copatulika; kuti angaone kanthu kodetsa mwa inu, ndi kukupotolokerani.

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 23