Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 22:18-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Pamenepo akuru a mudziwo azitenga munthuyu ndi kumkwapula;

19. ndi kumlipitsa masekeli makumi okha okha khumi a siliva, ndi kuipereka kwa atate wa namwaliyo, popeza anamveketsa dzina loipa namwali wa Israyeli, ndipo azikhala mkazi wace, sakhoza kumcotsa masiku ace onse.

20. Koma cikakhala coona ici, kuti zizindikilo zakuti ndiye namwali zidamsowa namwaliyo;

21. pamenepo azimturutsa namwaliyo ku khomo la nyumba ya atate wace, ndipo amuna a mudzi wace azimponya miyala kuti afe; popeza anacita copusa m'Israyeli, kucita cigololo m'nyumba ya atate wace; cotero uzicotsa coipaco pakati panu.

22. Akampeza munthu alikugona ndi mkazi wokwatibwa ndi mwamuna; afe onse awiri, mwamuna wakugona ndi mkazi, ndi mkazi yemwe; cotero muzicotsa coipaco mwa Israyeli.

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 22