Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 21:10-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Pamene muturuka kumka ku nkhondo ya pa adani anu, ndipo Yehova Mulungu wanu awapereka m'manja mwanu, ndipo muwagwira akhale akapolo anu;

11. mukaona mwa akapolowa mkazi wokongola, mukamkhumba, ndi kufuna kumtenga akhale mkazi wanu;

12. pamenepo mufike naye kwanu ku nyumba yanu; ndipo amete tsitsi la pamutu pace, ndi kuwenga makadabo ace;

13. nabvule zobvala za ukapolo wace, nakhale m'nyumba mwanu, nalire atate wace, ndi mai wace mwezi wamphumphu; ndipo atatero mulowe naye ndi kukhala mwamuna wace, ndi iye akhale mkazi wanu.

14. Ndipo kudzali, mukapanda kukondwera naye, mumlole apite komwe afuna; koma musamgulitsa ndalama konse, musamamuyesa cuma, popeza wamcepetsa.

15. Munthu akakhala nao akazi awiri, wina wokondana naye, wina wodana naye, nakambalira ana, wokondana naye, ndi wodana naye yemwe; ndipo mwana wamwamuna woyamba akakhala wa iye uja anadana naye;

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 21