4. Ndipo uuze anthu, ndi kuti, Mukapite kubzyola malire a abale anu, ana a Bsau okhala m'Seiri; ndipo adzakuopani; mucenjere ndithu;
5. musalimbana nao; popeza sindikupatsakoni dziko lao, pangakhale popondapo phazi lanu ai pakuti ndapatsa Bsau phiri la Seiri likhale lace lace.
6. Mugulane nao cakudya ndi ndarama, kuti mudye; mugulane naonso madzi kuti mumwe.