Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 2:28-33 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

28. Undigulitse cakudya ndi ndarama, kuti ndidye; ndi kundipatsa madzi kwa ndarama, kuti ndimwe; cokhaci ndipitire coyenda pansi;

29. monga anandicitira ana a Esau akukhala m'Seiri, ndi Amoabu akukhala m'Ari; kufikira nditaoloka Yordano kulowa dziko limene Yehova Mulungu wathu atipatsa.

30. Koma Sihoni mfumu ya Hesiboni sanatilola kupitira kwao; popeza Yehova Mulungu wanu anaumitsa mzimu wace, nalimbitsa mtima wace, kuti ampereke m'dzanja lanu, monga lero lino.

31. Ndipo Yehova anati kwa ine, Taona, ndayamba kupereka Sihoni ndi dziko lace pamaso pako; yamba kulandira dziko lace likhale lako lako.

32. Pamenepo Sihoni anaturuka kukomana nafe, iye ndi anthu ace onse, kugwirana nafe nkhondo ku Yahaza.

33. Ndipo Yehova Mulungu wathu anampereka iye pamaso pathu; ndipo tinamkantha, iye ndi ana ace amuna ndi anthu ace onse.

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 2