Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 2:13-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Ukani tsopano, olokani mtsinje wa Zeredi. Ndipo tinaoloka mtsinje wa Zeredi.

14. Ndipo masiku amene tinayenda kucokera ku Kadesi Barinea, kufikira tidaoloka mtsinje wa Zeredi, ndiwo zaka makumi atatu mphambu zisanu ndi zitatu; kufikira utatha mbadwo wonse wa amuna ankhondo m'cigono, monga Yehova adawalumbirira.

15. Komanso dzanja la Yehova linatsutsana nao, kuwaononga m'cigono, kufikira adawatha.

16. Ndipo kunali, atatha kufa amuna onse ankhondo mwa anthu,

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 2