Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 18:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ansembe Alevi, pfuko lonse la Levi, alibe gawo kapena colowa pamodzi ndi Israyeli; azizidya nsembe zamoto za Yehova, ndi colowa cace,

2. Alibe colowa pakati pa abale ao; Yehova mwini wace ndiye colowa cao, monga ananena nao.

3. Ndipo zoyenera ansembe, awapatse anthu akuphera nsembe ndizo: ingakhale ng'ombe kapena nkhosa azipatsa wansembe mwendo wamwamba, ndi ya m'masaya ndi chipfu.

4. Zipatso zoyamba za tirigu wanu, za vinyo wanu, ndi za mafuta anu ndi ubweya woyamba kuusenga, muwapatse izi.

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 18