Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 17:16-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Koma asadzicurukitsire akavalo iye, kapena kubwereretsa anthu amke ku Aigupto, kuti acurukitse akavalo; popeza Yehova anati nanu, Musamabwereranso njira iyi.

17. Ndipo asadzicurukitsire akazi, kuti ungapatuke mtinta wace; kapena asadzicurukitsire kwambiri siliva ndi golidi.

18. Ndipo kudzali, pakukhala iye pa mpando wacifumu wa ufumu wace, adzilemberere cofanana ca cilamuloici m'buku, acitenge pa ici ciri pamaso pa ansembe Alevi;

19. ndipo azikhala naco, nawerengemo masiku onse a moyo wace; kuti aphunzire kuopa Yehova Mulungu wace, kusunga mau ons acilamulo ici ndi malemba awa, kuwacita;

20. kuti mtima wace usadzikuze pa abaleace, ndi kuti asapatukire lamulolo, kulamanja kapena kulamanzere; kuti acuruke masiku ace, m'ufumu wace, iye ndi ana ace pakati pa Israyeli.

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 17