Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 17:1-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Musamaphera Yehova Mulungu wanu nsembe ya ng'ombe, kapena nkhosa, yokhala naco cirema, kapena ciri conse coipa; pakuti cinyansira Yehova Mulungu wanu.

2. Akapeza pakati panu, m'mudzi wanu wina umene anakupatsani Yehova Mulungu wanu, wamwamuna kapena wamkazi wakucita ciri coipa pamaso pa Yehova Mulungu wanu, ndi kulakwira cipangano cace,

3. nakatumikira milungu yina, naigwadira iyo, kapena dzuwa, kapena mwezi, kapena wina wa khamu la kuthambo, losauza Ine;

4. ndipo akakuuzani, nimudamva, pamenepo muzifunsitsa, ndipo taonani, cikakhala coonadi, coti nzenizeni, conyansaci cacitika m'Israyeli;

5. pamenepo muturutse mwamunayo kapena mkaziyo, anacita coipaco, kumka naye ku zipata zanu, ndiye wamwamuna kapena wamkazi; ndipo muwaponye miyala, kuti afe.

6. Pakamwa pa mboni ziwiri kapena zitatu amuphe iye amene akuti afe; asamuphe pakamwa pa mboni imodzi.

7. Liyambe kumgwera dzanja la mboniyo kumupha; pamenepo dzanja la anthu onse, Potero muzicotsa coipaco pakati panu.

8. Ukakulakani mlandu pouweruza, ndiwo wakunena zamwazi, kapena zakutsutsana, kapena zakupandana, ndiyo mirandu yakutengana m'midzi mwanu; pamenepo muziuka ndi kukwera kumka ku malo amene Yehova Mulungu wanu adzasankha;

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 17