Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 14:18-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. ndi iodwa, ndi cimeza, monga mwa mtundu wace, ndi sadzu, ndi mleme.

19. Ndipo zokwawa zonse zakuuluka muziyesa zonyansa; musamazidya.

20. Mbalame zonse zosadetsa muyenera kumadya.

21. Musamadya cinthu ciri conse citafa cokha; muzipereka ico kwa mlendo ali m'mudzi mwanu, acidye ndiye; kapena ucigulitse kwa mlendo; popeza ndinu mtundu wa anthu wopatulika wa Yehova Mulungu wanu. Musamaphika mwana wa mbuzi mu mkaka wa mace.

22. Muzipereka ndithu limodzi la magawo khumi la zipatso zonse za mbeu zanu, zofuma kumunda, caka ndi caka.

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 14