Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 11:27-32 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

27. dalitso, ngati mudzamvera malamulo a Yehova Mulungu wanu amene ndikuuzani lero lino;

28. koma temberero, ngati simudzamvera malamulo a Yehova Mulungu wanu, ndi kupatuka m'njira ndikuuzani lero lino, kutsata milungu yina imene simunaidziwa.

29. Ndipo kudzakhala, atakulowetsani Yehova Mulungu wanu m'dziko limene mumkako kulilandira, munene mdalitso pa phiri la Gerizimu, ndi temberero pa phiri la Ebala.

30. Sakhala kodi tsidya lija la Yordano, m'tseri mwace mwa njira yace yolowa dzuwa, m'dziko la Akanani, akukhala m'cidikha, pandunji pace pa Giligala, pafupi pa mathunda a More?

31. Pakuti mulinkuoloka Yordano kulowa ndi kulandira dziko limene Yehova Mulungu wanu akupatsani; ndipo mudzacilandira colowa canu, ndi kukhalamo.

32. Potero samalirani kucita malemba ndi maweruzo onse ndiwaika pamaso panu lero lino.

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 11