Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 1:42-46 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

42. Koma Yehova anati kwa ine, Nena nao, Musakwerako, kapena kuthira nkhondo; popeza sindiri pakati panu; angakukantheni adani anu.

43. Pamene ndinanena ndi inu simunamvera; koma munatsutsana nao mau a Yehova ndi kucita modzikuza, nimunakwera kumka kumapiri.

44. Ndipo Aamori, akukhala m'mapiri muja, anaturuka kukomana ndi inu, nakupitikitsani, monga zimacita njuci, nakukanthani m'Seiri, kufikira ku Horima.

45. Ndipo munabwerera ndi kulira pamaso pa Yehova; koma Yehova sanamvera mau anu, kapena kukucherani khutu.

46. Potero munakhala m'Kadesi masiku ambiri, monga mwa masiku munakhalako.

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 1