Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 1:38-41 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

38. Yoswa mwana wa Nuni, wakuima pamaso pako, iye adzalowamo; umlimbitse mtima; popeza iye adzalandiritsa Israyeli.

39. Ndipo ana anu amene mudanena, Adzakhala ogulidwa, ndi ana anu osadziwa cabwino kapena coipa ndi pano, iwo adzalowamo, ndidzawapatsa iwo ili, adzalilandira ndi iwo.

40. Koma inu, bwererani, mukani ulendo wanu kucipululu, njira ya ku Nyanja Yofiira.

41. Pamenepo munayankha ndi kunena ndi ine, Tacimwira Yehova, tidzakwera ndi kuthira mkhondo monga mwa zonse Yehova Mulungu wathu atiuza. Ndipo munadzimangira munthu yense zida zace za nkhondo, nimunakonzeka kukwera kumka kumapiri.

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 1