Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 1:36-46 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

36. Koma Kalebi mwana wa Yefune, iye adzaliona; ndidzampatsa iye dziko limene anapondapo, ndi ana ace; popeza analimbika ndi kutsata Yehova.

37. Yehova anakwiya ndi inenso cifukwa ca inu, ndi kuti, lwenso sudzalowamo.

38. Yoswa mwana wa Nuni, wakuima pamaso pako, iye adzalowamo; umlimbitse mtima; popeza iye adzalandiritsa Israyeli.

39. Ndipo ana anu amene mudanena, Adzakhala ogulidwa, ndi ana anu osadziwa cabwino kapena coipa ndi pano, iwo adzalowamo, ndidzawapatsa iwo ili, adzalilandira ndi iwo.

40. Koma inu, bwererani, mukani ulendo wanu kucipululu, njira ya ku Nyanja Yofiira.

41. Pamenepo munayankha ndi kunena ndi ine, Tacimwira Yehova, tidzakwera ndi kuthira mkhondo monga mwa zonse Yehova Mulungu wathu atiuza. Ndipo munadzimangira munthu yense zida zace za nkhondo, nimunakonzeka kukwera kumka kumapiri.

42. Koma Yehova anati kwa ine, Nena nao, Musakwerako, kapena kuthira nkhondo; popeza sindiri pakati panu; angakukantheni adani anu.

43. Pamene ndinanena ndi inu simunamvera; koma munatsutsana nao mau a Yehova ndi kucita modzikuza, nimunakwera kumka kumapiri.

44. Ndipo Aamori, akukhala m'mapiri muja, anaturuka kukomana ndi inu, nakupitikitsani, monga zimacita njuci, nakukanthani m'Seiri, kufikira ku Horima.

45. Ndipo munabwerera ndi kulira pamaso pa Yehova; koma Yehova sanamvera mau anu, kapena kukucherani khutu.

46. Potero munakhala m'Kadesi masiku ambiri, monga mwa masiku munakhalako.

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 1