Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 1:20-34 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. Ndipo ndinati kwa inu, Mwafikira mapiri a Aamori, amene Yehova Mulungu wathu atipatsa.

21. Taonani, Yehova Mulungu wanu wapatsa dzikoli pamaso panu; kwerakoni, landirani, monga Yehova Mulungu wa makolo anu, wanena ndi inu; musamacita mantha, musamatenga nkhawa.

22. Ndipo munayandikiza kwa ine inu nonse, ndi kuti, Titumize amuna atitsogolere, kuti akatizondere dziko ndi kutibwezera mau akunena za njira ya kukwera nayo ife pomka komweko, ndi za midzi yoti tidzafikako.

23. Ndipo cinandikomera cinthu ici; ndipo ndinatenga amuna khumi ndi awiri ainu, pfuko limodzi mwamuna mmodzi;

24. amenewa anatembenuka nakwera kumapiri nalowa ku cigwa ca Esikolo, nacizonda.

25. Ndipo anatengako zipatso za dzikoli m'manja mwao, natsikira nazo kwa ife, natibwezera mau ndi kuti, Dzikoli Yehova Mulungu wathu atipatsa ndi labwino.

26. Koma simunafuna kukwerako, ndipo munapikisana nao mau a Yehova Mulungu wanu.

27. Ndipo munadandaula m'mahema mwanu, ndi kuti, Popeza anatida Yehova, iye anatiturutsa m'dziko la Aigupto, kutipereka m'manja mwa Aamori, ationonge.

28. Tikwere kuti? abale athu atimyukitsa mitima yathu, ndi kuti, Anthuwo ndiwo akulu ndi atali akuposa ife; midzi ndi yaikulu ndi ya malinga ofikira m'mwamba: tinaonakonso ana a Anaki.

29. Pamenepo ndinati kwa inu, Musamaopsedwa, musamacita mantha nao.

30. Yehova Mulungu wanu wakutsogolera inu, iye adzathirira inu nkhondo, monga mwa zonse anakucitirani m'Aigupto pamaso panu;

31. ndi kucipululu, kumene munapenya kuti Yehova Mulungu wanu anakunyamulani, monga anyamula mwana wace wamwamuna, m'njira monse munayendamo, kufikira mutalowa m'malo muno.

32. Koma m'cinthu ici simunakhulupirira Yehova Mulungu wanu,

33. amene anakutsogolerani m'njira, kukufunirani malo akumanga mahema anu ndi mota usiku, kukuonetserani njira yoyendamo inu, ndi mumtambo usana.

34. Ndipo Yehova anamva mau a kunena kwanu, nakwiya, nalumbira, ndi kuti,

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 1